Yemwe amayankhulapo pankhani zosiyanasiya zochitika m’dziko muno a Francis Liyati, adzuzura akulu akulu a zamaphunziro m’boma la Mzimba posalabadira ndi kuthana ndi nkhani za nkhanza zomwe m’phunzitsi wa mkulu pa sukulu ya Mzimba LEA Joseph Chirwa akuchitira aphunzitsi achizimai.