Achinyamata khumi ndi awiri omwe anayiwala kuti ukayendera n’zengo usati asakhwi afumbura, awathamangitsa m’dziko la Israel kamba kotaya chingamu chifukwa cha mtedza olawa. Sabata latha, a Polisi m’dzikolo anamanga achinyamata okwana makumi anayi ndi mphambu zisanu chifukwa chothawa ntchito zosiyanasiyana zomwe anapitira m’dzikolo ndikupita kukayamba ntchito ku kampani zina m’dziko momwemo.